Números 33
Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs NTLH
1 Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni.
1 São estas as caminhadas dos israelitas que saíram do Egito, grupo por grupo, debaixo das ordens de Moisés e Arão.
2 Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:
2 Moisés ia anotando os nomes dos lugares de onde partiam, de acordo com as ordens de Deus, o Senhor . E são estas as caminhadas conforme os lugares de partida:
3 Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona,
3 O povo de Israel saiu do Egito no dia quinze do primeiro mês do ano, um dia depois da primeira Páscoa . Eles saíram de Ramessés de maneira vitoriosa, e todos os egípcios os viram.
4 pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.
4 Os egípcios estavam sepultando os seus primeiros filhos que o Senhor havia matado. Assim, o Senhor mostrou que era mais poderoso do que os deuses do Egito.
5 Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.
5 Depois de saírem de Ramessés, os israelitas acamparam em Sucote.
6 Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.
6 Saíram de Sucote e acamparam em Etã, que está na beira do deserto.
7 Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.
7 Saíram de Etã e voltaram a Pi-Hairote, que fica a leste de Baal-Zefom, e acamparam perto de Migdol.
8 Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.
8 Saíram de Pi-Hairote e passaram pelo meio do mar Vermelho e chegaram ao deserto de Sur. Caminharam três dias no deserto e acamparam em Mara.
9 Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.
9 Dali foram para Elim e acamparam ali. Em Elim havia doze fontes de água e setenta palmeiras.
10 Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.
10 Saíram de Elim e acamparam perto do golfo de Suez.
11 Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.
11 Partiram dali e acamparam no deserto de Sim.
12 Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.
12 Dali foram até Dofca, onde acamparam.
13 Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.
13 Partiram de Dofca e acamparam em Alus.
14 Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.
14 Depois de Alus, acamparam em Refidim. Porém ali não havia água para o povo beber.
15 Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai
15 — ausente —
16 Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.
16 — ausente —
17 Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.
17 — ausente —
18 Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.
18 — ausente —
19 Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.
19 — ausente —
20 Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.
20 — ausente —
21 Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.
21 — ausente —
22 Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.
22 — ausente —
23 Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.
23 — ausente —
24 Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.
24 — ausente —
25 Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.
25 — ausente —
26 Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.
26 — ausente —
27 Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.
27 — ausente —
28 Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.
28 — ausente —
29 Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.
29 — ausente —
30 Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.
30 — ausente —
31 Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.
31 — ausente —
32 Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.
32 — ausente —
33 Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.
33 — ausente —
34 Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.
34 — ausente —
35 Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.
35 — ausente —
36 Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.
36 — ausente —
37 Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu.
37 — ausente —
38 Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.
38 Por ordem de Deus, o Senhor , o sacerdote Arão subiu o monte Hor. E morreu ali, no dia primeiro do quinto mês, quarenta anos depois que os israelitas tinham saído do Egito.
39 Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.
39 Arão tinha cento e vinte e três anos de idade quando morreu.
40 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.
40 Então o rei cananeu de Arade, que morava na região sul da terra de Canaã, soube que os israelitas estavam chegando.
41 Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.
41 — ausente —
42 Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.
42 — ausente —
43 Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.
43 — ausente —
44 Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.
44 — ausente —
45 Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.
45 — ausente —
46 Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.
46 — ausente —
47 Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.
47 — ausente —
48 Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
48 — ausente —
49 Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.
49 — ausente —
50 Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti,
50 Nas planícies de Moabe, junto ao rio Jordão, na altura de Jericó, que ficava no outro lado do rio, o Senhor mandou que Moisés desse
51 “Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani,
51 aos israelitas as seguintes ordens: — Quando vocês atravessarem o rio Jordão e entrarem na terra de Canaã,
52 mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo.
52 expulsem todos os moradores daquela terra. Destruam todos os seus ídolos de metal e de pedra e todos os seus lugares de adoração.
53 Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo.
53 Tomem posse da terra e morem nela porque eu a estou dando a vocês.
54 Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.
54 Repartam a terra, por sorteio , entre as tribos e os grupos de famílias. Aos grupos de famílias mais numerosos deem uma parte maior; e aos grupos menos numerosos deem uma parte menor.
55 “ ‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo.
55 Porém, se vocês não expulsarem os moradores do país, os que ficarem serão para vocês como espinhos nos seus olhos e como ferrões nas suas costas e trarão problemas para vocês na terra em que vocês morarem.
56 Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’ ”
56 E farei com vocês tudo o que eu havia pensado fazer com eles.
Atalhos do teclado
- Capítulo anterior←
- Próximo capítulo→
- Versículo anteriork
- Próximo versículoj
- Limpar seleçãoEsc
- Esta ajuda?
Estude este capítulo no WhatsApp
Peça à IA da Bíblia Fala para explicar Números 33, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.