Deuteronômio 14

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs ARA

Sair da comparação
ARA Almeida Revista e Atualizada 1993
1 Inu ndinu ana a Yehova Mulungu wanu. Osamadzichekacheka kapena kudzimeta pamphumi chifukwa cha abale anu amene amwalira,
1 Filhos sois do Senhor , vosso Deus; não vos dareis golpes, nem sobre a testa fareis calva por causa de algum morto.
2 pakuti ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu. Pakati pa anthu onse pa dziko lonse lapansi, Yehova wasankha inu kuti chikhale chuma chake chamtengo wapatali.
2 Porque sois povo santo ao Senhor , vosso Deus, e o Senhor vos escolheu de todos os povos que há sobre a face da terra, para lhe serdes seu povo próprio.
3 Musamadye chinthu chilichonse chonyansa.
3 Não comereis coisa alguma abominável.
4 Nyama zomwe mukhoza kudya ndi izi: ngʼombe, nkhosa, mbuzi,
4 São estes os animais que comereis: o boi, a ovelha, a cabra,
5 mbawala, gwape, mphoyo, mphalapala, ngoma, nyumbu ndi mbalale.
5 o veado, a gazela, a corça, a cabra montês, o antílope, a ovelha montês e o gamo.
6 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
6 Todo animal que tem unhas fendidas, e o casco se divide em dois, e rumina, entre os animais, isso comereis.
7 Komabe pakati pa nyama zimene zimabzikula kapena zogawikana zipondero, zimene simukuyenera kudya ndi ngamira, kalulu ndi mbira. Zimenezi ngakhale zimabzikula, zipondero zake sizogawikana, choncho ndi zodetsedwa, musadye.
7 Porém estes não comereis, dos que somente ruminam ou que têm a unha fendida: o camelo, a lebre e o arganaz, porque ruminam, mas não têm a unha fendida; imundos vos serão.
8 Nkhumba simabzikula ndi yodetsedwanso ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa.
8 Nem o porco, porque tem unha fendida, mas não rumina; imundo vos será. Destes não comereis a carne e não tocareis no seu cadáver.
9 Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi, mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
9 Isto comereis de tudo o que há nas águas: tudo o que tem barbatanas e escamas.
10 Koma chilichonse chimene chilibe minga ya pa msana ndi mamba musadye pakuti nʼchodetsedwa.
10 Mas tudo o que não tiver barbatanas nem escamas não o comereis; imundo vos será.
11 Mukhoza kudya mbalame iliyonse yoyenera kudya.
11 Toda ave limpa comereis.
12 Koma simukuyenera kudya izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
12 Estas, porém, são as que não comereis: a águia, o quebrantosso, a águia marinha,
13 nankapakapa, akamtema, akhungubwi a mitundu yonse, ndi mtundu uliwonse wa miphamba,
13 o açor, o falcão e o milhano, segundo a sua espécie;
14 mtundu uliwonse wa khwangwala,
14 e todo corvo, segundo a sua espécie;
15 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo, mtundu uliwonse wa akabawi,
15 o avestruz, a coruja, a gaivota e o gavião, segundo a sua espécie;
16 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
16 o mocho, a íbis, a gralha,
17 tsekwe, vuwo, dembo,
17 o pelicano, o abutre, o corvo marinho,
18 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
18 a cegonha, e a garça, segundo a sua espécie, e a poupa, e o morcego.
19 Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa. Musamadye zimenezi.
19 Também todo inseto que voa vos será imundo; não se comerá.
20 Koma chowuluka chilichonse choyenera kudya mukhoza kudya.
20 Toda ave limpa comereis.
21 Musamadye chilichonse chimene mwachipeza chofaifa. Mukhoza kupatsa mlendo amene akukhala mu mzinda wina uliwonse wa mizinda yanu. Iyeyo akhoza kudya kapena mukhoza kugulitsa kwa wina aliyense amene sali wa mtundu wanu. Koma inu ndinu anthu opatulika a Yehova Mulungu wanu.
21 Não comereis nenhum animal que morreu por si. Podereis dá-lo ao estrangeiro que está dentro da tua cidade, para que o coma, ou vendê-lo ao estranho, porquanto sois povo santo ao Senhor , vosso Deus. Não cozerás o cabrito no leite da sua própria mãe.
22 Muzionetsetsa kuti mukupatula chakhumi pa zokolola zanu chaka chilichonse.
22 Certamente, darás os dízimos de todo o fruto das tuas sementes, que ano após ano se recolher do campo.
23 Muzidyera chakhumi cha tirigu wanu, vinyo wanu watsopano ndi mafuta, ndi ana oyamba kubadwa a ngʼombe zanu pamaso pa Yehova Mulungu wanu pa malo amene adzasankhe ngati kokhalako dzina lake, kuti muphunzire kuopa Yehova Mulungu wanu.
23 E, perante o Senhor , teu Deus, no lugar que escolher para ali fazer habitar o seu nome, comerás os dízimos do teu cereal, do teu vinho, do teu azeite e os primogênitos das tuas vacas e das tuas ovelhas; para que aprendas a temer o Senhor , teu Deus, todos os dias.
24 Koma ngati malo amenewa ali kutali kwambiri ndipo kuti inu mwadalitsidwa ndi Yehova Mulungu wanu, ndipo simungathe kunyamula chakhumi chanu (chifukwa chakuti malo amene Yehova adzasankha kukayikako dzina lake ali kutali kwambiri),
24 Quando o caminho te for comprido demais, que os não possas levar, por estar longe de ti o lugar que o Senhor , teu Deus, escolher para ali pôr o seu nome, quando o Senhor , teu Deus, te tiver abençoado,
25 ndiye musinthitse chakhumi chanucho ndi siliva, ndipo mutenge silivayo ndi kupita naye kumalo kumene Yehova Mulungu wanu adzasankhe.
25 então, vende-os, e leva o dinheiro na tua mão, e vai ao lugar que o Senhor , teu Deus, escolher.
26 Gwiritsani ntchito silivayo kugula chilichonse chimene muchifuna monga ngʼombe, nkhosa, vinyo kapena zakumwa zina zosasitsa, kapena china chilichonse chimene muchifuna. Ndipo inu ndi anthu a pa banja panu mudzazidyera komweko pamaso pa Yehova Mulungu wanu ndi kukondwera.
26 Esse dinheiro, dá-lo-ás por tudo o que deseja a tua alma, por vacas, ou ovelhas, ou vinho, ou bebida forte, ou qualquer coisa que te pedir a tua alma; come-o ali perante o Senhor , teu Deus, e te alegrarás, tu e a tua casa;
27 Alevi okhala mʼmizinda yanu musaleke kuwathandiza popeza alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo.
27 porém não desampararás o levita que está dentro da tua cidade, pois não tem parte nem herança contigo.
28 Kumapeto kwa zaka zitatu zilizonse muzibweretsa zakhumi zonse pa zokolola za chaka chimenecho ndi kuzisunga mʼmidzi yanu,
28 Ao fim de cada três anos, tirarás todos os dízimos do fruto do terceiro ano e os recolherás na tua cidade.
29 kuti Alevi (amene alibe gawo lawo la chuma kapena cholowa chawochawo), alendo, ana ndi akazi amasiye, amene akukhala mʼmizinda yanu akhoza kubwera kudzadya ndi kukhuta. Ndipo kuti akutero Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa ntchito zanu zonse.
29 Então, virão o levita (pois não tem parte nem herança contigo), o estrangeiro, o órfão e a viúva que estão dentro da tua cidade, e comerão, e se fartarão, para que o Senhor , teu Deus, te abençoe em todas as obras que as tuas mãos fizerem.

Ler em outra tradução

Comparar com outra

Estude este capítulo no WhatsApp

Peça à IA da Bíblia Fala para explicar Deuteronômio 14, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.