1 Tessalonicenses 5
Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs NVI
1 Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni,
1 Irmãos, quanto aos tempos e épocas, não precisamos escrever-lhes,
2 chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku.
2 pois vocês mesmos sabem perfeitamente que o dia do Senhor virá como ladrão à noite.
3 Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.
3 Quando disserem: "Paz e segurança", então, de repente, a destruição virá sobre eles, como dores à mulher grávida; e de modo nenhum escaparão.
4 Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala.
4 Mas vocês, irmãos, não estão nas trevas, para que esse dia os surpreenda como ladrão.
5 Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima.
5 Vocês todos são filhos da luz, filhos do dia. Não somos da noite nem das trevas.
6 Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga.
6 Portanto, não durmamos como os demais, mas estejamos atentos e sejamos sóbrios;
7 Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku.
7 pois os que dormem, dormem de noite, e os que se embriagam, embriagam-se de noite.
8 Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa.
8 Nós, porém, que somos do dia, sejamos sóbrios, vestindo a couraça da fé e do amor e o capacete da esperança da salvação.
9 Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
9 Porque Deus não nos destinou para a ira, mas para recebermos a salvação por meio de nosso Senhor Jesus Cristo.
10 Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi.
10 Ele morreu por nós para que, quer estejamos acordados quer dormindo, vivamos unidos a ele.
11 Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.
11 Por isso, exortem-se e edifiquem-se uns aos outros, como de fato vocês estão fazendo.
12 Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani.
12 Agora lhes pedimos, irmãos, que tenham consideração para com os que se esforçam no trabalho entre vocês, que os lideram no Senhor e os aconselham.
13 Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.
13 Tenham-nos na mais alta estima, com amor, por causa do trabalho deles. Vivam em paz uns com os outros.
14 Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense.
14 Exortamos vocês, irmãos, a que advirtam os ociosos, confortem os desanimados, auxiliem os fracos, sejam pacientes para com todos.
15 Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.
15 Tenham cuidado para que ninguém retribua o mal com o mal, mas sejam sempre bondosos uns para com os outros e para com todos.
16 Kondwerani nthawi zonse.
16 Alegrem-se sempre.
17 Pempherani kosalekeza.
17 Orem continuamente.
18 Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.
18 Dêem graças em todas as circunstâncias, pois esta é a vontade de Deus para vocês em Cristo Jesus.
19 Musazimitse moto wa Mzimu Woyera.
19 Não apaguem o Espírito.
20 Musanyoze mawu a uneneri.
20 Não tratem com desprezo as profecias,
21 Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino.
21 mas ponham à prova todas as coisas e fiquem com o que é bom.
22 Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.
22 Afastem-se de toda forma de mal.
23 Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu.
23 Que o próprio Deus da paz os santifique inteiramente. Que todo o espírito, alma e corpo de vocês seja conservado irrepreensível na vinda de nosso Senhor Jesus Cristo.
24 Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.
24 Aquele que os chama é fiel, e fará isso.
25 Abale, mutipempherere.
25 Irmãos, orem por nós.
26 Perekani moni wachikondi kwa onse.
26 Saúdem todos os irmãos com beijo santo.
27 Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.
27 Responsabilizo-os diante do Senhor para que esta carta seja lida a todos os irmãos.
28 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.
28 A graça de nosso Senhor Jesus Cristo seja com vocês.
Atalhos do teclado
- Capítulo anterior←
- Próximo capítulo→
- Versículo anteriork
- Próximo versículoj
- Limpar seleçãoEsc
- Esta ajuda?
Estude este capítulo no WhatsApp
Peça à IA da Bíblia Fala para explicar 1 Tessalonicenses 5, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.