1 Tessalonicenses 5

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs NAA

Sair da comparação
NAA Nova Almeida Atualizada 2017
1 Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni,
1 Irmãos, no que se refere aos tempos e às épocas, não há necessidade de que eu lhes escreva.
2 chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku.
2 Porque vocês sabem perfeitamente que o Dia do Senhor vem como ladrão à noite.
3 Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.
3 Quando andarem dizendo: “Paz e segurança”, eis que lhes sobrevirá repentina destruição, como vêm as dores de parto à mulher que está para dar à luz; e de modo nenhum escaparão.
4 Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala.
4 Mas vocês, irmãos, não estão em trevas, para que esse Dia os apanhe de surpresa como ladrão.
5 Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima.
5 Porque vocês todos são filhos da luz e filhos do dia; nós não somos da noite, nem das trevas.
6 Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga.
6 Assim, pois, não durmamos como os demais; pelo contrário, vigiemos e sejamos sóbrios.
7 Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku.
7 Ora, os que dormem é de noite que dormem, e os que se embriagam é de noite que se embriagam.
8 Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa.
8 Nós, porém, que somos do dia, sejamos sóbrios, revestindo-nos da couraça da fé e do amor e tomando como capacete a esperança da salvação.
9 Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu.
9 Porque Deus não nos destinou para a ira, mas para alcançar a salvação mediante nosso Senhor Jesus Cristo,
10 Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi.
10 que morreu por nós para que, quer vigiemos, quer durmamos, vivamos em união com ele.
11 Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.
11 Portanto, consolem uns aos outros e edifiquem-se mutuamente, como vocês têm feito até agora.
12 Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani.
12 Irmãos, pedimos que vocês tenham em grande apreço os que trabalham entre vocês, que os presidem no Senhor e os admoestam.
13 Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake.
13 Tenham essas pessoas em máxima consideração, com amor, por causa do trabalho que realizam. Vivam em paz uns com os outros.
14 Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense.
14 Também exortamos vocês, irmãos, a que admoestem os que vivem de forma desordenada, consolem os desanimados, amparem os fracos e sejam pacientes com todos.
15 Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.
15 Tenham cuidado para que ninguém retribua aos outros mal por mal; pelo contrário, procurem sempre o bem uns dos outros e o bem de todos.
16 Kondwerani nthawi zonse.
16 Estejam sempre alegres.
17 Pempherani kosalekeza.
17 Orem sem cessar.
18 Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.
18 Em tudo, deem graças, porque esta é a vontade de Deus para vocês em Cristo Jesus.
19 Musazimitse moto wa Mzimu Woyera.
19 Não apaguem o Espírito.
20 Musanyoze mawu a uneneri.
20 Não desprezem as profecias.
21 Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino.
21 Examinem todas as coisas, retenham o que é bom.
22 Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.
22 Abstenham-se de toda forma de mal.
23 Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu.
23 O mesmo Deus da paz os santifique em tudo. E que o espírito, a alma e o corpo de vocês sejam conservados íntegros e irrepreensíveis na vinda de nosso Senhor Jesus Cristo.
24 Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.
24 Fiel é aquele que os chama, o qual também o fará.
25 Abale, mutipempherere.
25 Irmãos, orem também por nós.
26 Perekani moni wachikondi kwa onse.
26 Saúdem todos os irmãos com um beijo santo.
27 Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.
27 Peço, com insistência, em nome do Senhor, que esta carta seja lida para todos os irmãos.
28 Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.
28 A graça de nosso Senhor Jesus Cristo esteja com vocês!

Ler em outra tradução

Comparar com outra

Estude este capítulo no WhatsApp

Peça à IA da Bíblia Fala para explicar 1 Tessalonicenses 5, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.