1 Timóteo 2
Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs NAA
1 Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika.
1 Antes de tudo, peço que se façam súplicas, orações, intercessões e ações de graças em favor de todas as pessoas.
2 Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima.
2 Orem em favor dos reis e de todos os que exercem autoridade, para que vivamos vida mansa e tranquila, com toda piedade e respeito.
3 Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu,
3 Isto é bom e aceitável diante de Deus, nosso Salvador,
4 amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi.
4 que deseja que todos sejam salvos e cheguem ao pleno conhecimento da verdade.
5 Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu.
5 Porque há um só Deus e um só Mediador entre Deus e a humanidade, Cristo Jesus, homem,
6 Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera.
6 que deu a si mesmo em resgate por todos, testemunho que se deve dar em tempos oportunos.
7 Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.
7 Para isto fui designado pregador e apóstolo — afirmo a verdade, não minto —, mestre dos gentios na fé e na verdade.
8 Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.
8 Quero, pois, que os homens orem em todos os lugares, levantando mãos santas, sem ira e sem animosidade.
9 Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali.
9 Da mesma forma, que as mulheres, em traje decente, se enfeitem com modéstia e bom senso, não com tranças no cabelo, ouro, pérolas ou roupas caras,
10 Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.
10 porém com boas obras, como convém a mulheres que professam ser piedosas.
11 Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu.
11 A mulher aprenda em silêncio, com toda a submissão.
12 Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete.
12 E não permito que a mulher ensine, nem que exerça autoridade sobre o homem; esteja, porém, em silêncio.
13 Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava.
13 Porque primeiro foi formado Adão, depois Eva.
14 Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa.
14 E Adão não foi iludido, mas a mulher, sendo enganada, caiu em transgressão.
15 Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.
15 Mas ela será salva tendo filhos, se permanecer em fé, amor e santificação, com bom senso.
Atalhos do teclado
- Capítulo anterior←
- Próximo capítulo→
- Versículo anteriork
- Próximo versículoj
- Limpar seleçãoEsc
- Esta ajuda?
Estude este capítulo no WhatsApp
Peça à IA da Bíblia Fala para explicar 1 Timóteo 2, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.