1 Timóteo 2

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs BKJ

Sair da comparação
1 Tsono choyamba ndikukupemphani kuti mupempherere anthu onse. Mapemphero anu akhale opemba, opempha, opempherera ena ndi oyamika.
1 Exorto-te que antes de tudo se façam súplicas, orações, intercessões e ações de graças por todos os homens,
2 Mupempherere mafumu ndi onse aulamuliro, kuti tikhale moyo wamtendere ndi bata, woopa Mulungu ndi oyera mtima.
2 pelos reis e por todos os que estão em autoridade, para que tenhamos uma vida quieta e sossegada, em toda a piedade e honestidade.
3 Izi ndi zabwino ndipo zimakondweretsa Mulungu Mpulumutsi wathu,
3 Porque isto é bom e aceitável aos olhos de Deus, nosso Salvador,
4 amene amafuna kuti anthu onse apulumutsidwe ndipo kuti adziwe choonadi.
4 que quer que todos os homens se salvem e venham ao conhecimento da verdade.
5 Pakuti pali Mulungu mmodzi yekha ndi Mʼkhalapakati mmodzi yekha pakati pa Mulungu ndi anthu, munthu uja Khristu Yesu.
5 Porque há um só Deus e um só mediador entre Deus e os homens, o homem Jesus Cristo,
6 Iyeyu anadzipereka kukhala dipo lowombolera anthu onse. Umenewu ndi umboni umene waperekedwa mu nthawi yake yoyenera.
6 o qual se entregou a si mesmo como resgate por todos, para servir de testemunho a seu tempo.
7 Nʼchifukwa chake anandisankha kukhala mlaliki ndiponso mtumwi wophunzitsa anthu a mitundu ina mawu achikhulupiriro choona. Sindikunama ayi, ndikunena zoona.
7 Para o que fui constituído pregador, e um apóstolo (digo a verdade em Cristo e não minto), e mestre dos gentios na fé e na verdade.
8 Choncho ndikufuna kuti paliponse popemphera, amuna azikweza manja awo kwa Mulungu mopanda mkwiyo kapena kukangana.
8 Quero, pois, que os homens orem em todo o lugar, levantando mãos santas, sem ira nem dúvida.
9 Ndikufunanso kuti amayi azivala mwaulemu, modzilemekeza ndi moyenera. Adzikongoletse koma osati ndi tsitsi loluka mowonjeza muyeso kapena zokongoletsa zagolide kapena mikanda yamtengowapatali kapena ndi zovala zamtengowapatali.
9 Que do mesmo modo as mulheres se ataviem em vestuário modesto, com pudor e sobriedade, não com tranças, ou ouro, ou pérolas, ou vestidos dispendiosos,
10 Koma adzikongoletse ndi ntchito zabwino zoyenera mayi wopembedza Mulungu.
10 mas (como convém a mulheres que professam a piedade) com boas obras.
11 Amayi azikhala chete pophunzitsidwa ndi mtima ogonjera kwathunthu.
11 A mulher aprenda em silêncio, com toda a sujeição.
12 Ine sindikulola kuti amayi aziphunzitsa kapena kulamulira amuna; koma akhale chete.
12 Mas não permito que a mulher ensine, nem usurpe a autoridade do homem, mas que esteja em silêncio.
13 Pakuti Adamu ndiye anayamba kupangidwa kenaka Hava.
13 Porque Adão foi formado primeiro, depois Eva.
14 Ndipo Adamu si amene ananyengedwa koma mkazi ndiye amene ananyengedwa nachimwa.
14 E Adão não foi enganado, mas a mulher, sendo enganada, caiu em transgressão.
15 Ndipo mkazi adzapulumutsidwa pobereka mwana ngati apitiriza kukhala mʼchikhulupiriro, mʼchikondi ndi mʼkuyera mtima pamodzi ndi kudzichepetsa konse.
15 Contudo ela será salva, dando à luz filhos, se continuar na fé e caridade, e santidade com sobriedade.

Ler em outra tradução

Comparar com outra

Estude este capítulo no WhatsApp

Peça à IA da Bíblia Fala para explicar 1 Timóteo 2, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.