Mateus 22

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs ARA

Sair da comparação
ARA Almeida Revista e Atualizada 1993
1 Yesu anayankhula nawonso mʼmafanizo, nati,
1 De novo, entrou Jesus a falar por parábolas, dizendo-lhes:
2 “Ufumu wakumwamba uli ngati mfumu imene inakonzera phwando mwana wake wamwamuna.
2 O reino dos céus é semelhante a um rei que celebrou as bodas de seu filho.
3 Anatumiza antchito ake kwa amene anayitanidwa kuphwando koma anakana kubwera.
3 Então, enviou os seus servos a chamar os convidados para as bodas; mas estes não quiseram vir.
4 “Kenaka anatumiza antchito ena nati, ‘Awuzeni oyitanidwa kuti phwando lakonzedwa: ndapha ngʼombe yayimuna ndi nyama zina zonenepa ndipo zonse zakonzedwa. Bwerani ku phwando laukwati.’
4 Enviou ainda outros servos, com esta ordem: Dizei aos convidados: Eis que já preparei o meu banquete; os meus bois e cevados já foram abatidos, e tudo está pronto; vinde para as bodas.
5 “Koma iwo sanalabadire ndipo anachoka; wina anapita ku munda wake ndi wina ku malonda ake.
5 Eles, porém, não se importaram e se foram, um para o seu campo, outro para o seu negócio;
6 Ndipo otsalawo anagwira antchito ake, nawazunza ndi kuwapha.
6 e os outros, agarrando os servos, os maltrataram e mataram.
7 Mfumu inakwiya. Inatumiza asilikali ake ndipo anawononga opha anzawowo ndi kutentha mzinda wawo.
7 O rei ficou irado e, enviando as suas tropas, exterminou aqueles assassinos e lhes incendiou a cidade.
8 “Pamenepo anati kwa antchito ake, ‘Phwando laukwati lakonzedwa, koma amene ndinawayitana sanali oyenera.
8 Então, disse aos seus servos: Está pronta a festa, mas os convidados não eram dignos.
9 Pitani ku mphambano za misewu ndipo kayitaneni aliyense amene mukamupeze kuti abwere ku phwando.’
9 Ide, pois, para as encruzilhadas dos caminhos e convidai para as bodas a quantos encontrardes.
10 Pamenepo antchitowo anapita ku misewu nakasonkhanitsa anthu onse amene anakawapeza, abwino ndi oyipa omwe, ndipo nyumba ya madyerero inadzaza ndi oyitanidwa.
10 E, saindo aqueles servos pelas estradas, reuniram todos os que encontraram, maus e bons; e a sala do banquete ficou repleta de convidados.
11 “Koma pamene mfumu inabwera kudzaona oyitanidwawo, inaona munthu amene sanavale zovala zaukwati.
11 Entrando, porém, o rei para ver os que estavam à mesa, notou ali um homem que não trazia veste nupcial
12 Inamufunsa kuti, ‘Bwenzi walowa bwanji muno wopanda zovala zaukwati?’ Munthuyo anakhala chete.
12 e perguntou-lhe: Amigo, como entraste aqui sem veste nupcial? E ele emudeceu.
13 “Pamenepo mfumuyo inawuza otumikira kuti, ‘Mʼmangeni manja ndi miyendo, ndipo muponyeni kunja, ku mdima kumene kudzakhale kulira ndi kukuta mano.’
13 Então, ordenou o rei aos serventes: Amarrai-o de pés e mãos e lançai-o para fora, nas trevas; ali haverá choro e ranger de dentes.
14 “Popeza oyitanidwa ndi ambiri koma osankhidwa ndi ochepa.”
14 Porque muitos são chamados, mas poucos, escolhidos.
15 Kenaka Afarisi anatuluka nakakonza njira zomupezera zifukwa Yesu mʼmawu ake.
15 Então, retirando-se os fariseus, consultaram entre si como o surpreenderiam em alguma palavra.
16 Anatumiza ophunzira awo kwa Iye pamodzi ndi Aherodia. Anati, “Aphunzitsi, tidziwa kuti ndinu wangwiro ndi kuti mumaphunzitsa mawu a Mulungu monga mwa choonadi. Simutekeseka ndi anthu, popeza simusamala kuti kodi ndi ndani?
16 E enviaram-lhe discípulos, juntamente com os herodianos, para dizer-lhe: Mestre, sabemos que és verdadeiro e que ensinas o caminho de Deus, de acordo com a verdade, sem te importares com quem quer que seja, porque não olhas a aparência dos homens.
17 Tiwuzeni tsono maganizo anu ndi otani, kodi nʼkololedwa kupereka msonkho kwa Kaisara kapena ayi?”
17 Dize-nos, pois: que te parece? É lícito pagar tributo a César ou não?
18 Koma Yesu podziwa maganizo awo oyipa anati, “Inu achiphamaso, bwanji mufuna kundipezera chifukwa?
18 Jesus, porém, conhecendo-lhes a malícia, respondeu: Por que me experimentais, hipócritas?
19 Onetseni ndalama imene mumapereka msonkho.” Iwo anabweretsa dinari,
19 Mostrai-me a moeda do tributo. Trouxeram-lhe um denário.
20 ndipo anawafunsa kuti, “Kodi chithunzi ichi ndi malemba awa ndi za ndani?”
20 E ele lhes perguntou: De quem é esta efígie e inscrição?
21 Iwo anayankha kuti, “Ndi za Kaisara.”
21 Responderam: De César. Então, lhes disse: Dai, pois, a César o que é de César e a Deus o que é de Deus.
22 Atamva izi, anadabwa, ndipo anamusiya Iye, nachoka.
22 Ouvindo isto, se admiraram e, deixando-o, foram-se.
23 Tsiku lomwelo Asaduki amene amati kulibe za kuukanso, anabwera kwa Iye ndi funso.
23 Naquele dia, aproximaram-se dele alguns saduceus, que dizem não haver ressurreição, e lhe perguntaram:
24 Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatiwuza kuti munthu akamwalira wosasiya ana, mʼbale wake akuyenera kukwatira mkazi wamasiyeyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
24 Mestre, Moisés disse: Se alguém morrer, não tendo filhos, seu irmão casará com a viúva e suscitará descendência ao falecido.
25 Tsopano panali abale asanu ndi awiri pakati pathu. Woyambayo anakwatira ndipo anamwalira, ndipo popeza analibe ana, mʼbale wake analowa chokolo.
25 Ora, havia entre nós sete irmãos. O primeiro, tendo casado, morreu e, não tendo descendência, deixou sua mulher a seu irmão;
26 Izi zinachitikiranso mʼbale wa chiwiri ndi wachitatu mpaka wachisanu ndi chiwiri.
26 o mesmo sucedeu com o segundo, com o terceiro, até ao sétimo;
27 Pa mapeto pake mkaziyo anamwaliranso.
27 depois de todos eles, morreu também a mulher.
28 Tsopano, kodi akadzaukitsidwa adzakhala mkazi wa ndani mwa asanu ndi awiriwa popeza aliyense anamukwatirapo?”
28 Portanto, na ressurreição, de qual dos sete será ela esposa? Porque todos a desposaram.
29 Yesu anayankha kuti, “Inu mukulakwitsa chifukwa simukudziwa malemba kapena mphamvu ya Mulungu.
29 Respondeu-lhes Jesus: Errais, não conhecendo as Escrituras nem o poder de Deus.
30 Anthu akadzaukitsidwa, sadzakwatira kapena kukwatiwa; adzakhala ngati angelo kumwamba.
30 Porque, na ressurreição, nem casam, nem se dão em casamento; são, porém, como os anjos no céu.
31 Koma za kuukitsidwa kwa akufa, kodi simunawerenge zimene Mulungu ananena kwa inu kuti,
31 E, quanto à ressurreição dos mortos, não tendes lido o que Deus vos declarou:
32 ‘Ine ndine Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo?’ Iyeyo si Mulungu wa akufa koma wa amoyo.”
32 Eu sou o Deus de Abraão, o Deus de Isaque e o Deus de Jacó?
33 Magulu a anthu atamva zimenezi, anazizwa ndi chiphunzitso chake.
33 Ouvindo isto, as multidões se maravilhavam da sua doutrina.
34 Pakumva kuti Yesu anawakhalitsa chete Asaduki, Afarisi anasonkhana pamodzi.
34 Entretanto, os fariseus, sabendo que ele fizera calar os saduceus, reuniram-se em conselho.
35 Mmodzi wa iwo, katswiri wa malamulo anamuyesa Iye ndi funso ndipo anati,
35 E um deles, intérprete da Lei, experimentando-o, lhe perguntou:
36 “Aphunzitsi, kodi lamulo lalikulu koposa mu malamulo ndi liti?”
36 Mestre, qual é o grande mandamento na Lei?
37 Yesu anayankha kuti, “Uzikonda Yehova Mulungu wako ndi mtima wako wonse ndi moyo wako wonse ndi nzeru zako zonse.
37 Respondeu-lhe Jesus:
38 Ili ndi lamulo loyamba ndi loposa onse.
38 Este é o grande e primeiro mandamento.
39 Ndipo lachiwiri ndi lofanana nalo: ‘Konda mnansi wako monga iwe mwini.’
39 O segundo, semelhante a este, é:
40 Malamulo onse ndi aneneri zakhazikika pa malamulo awiriwa.”
40 Destes dois mandamentos dependem toda a Lei e os Profetas.
41 Afarisi atasonkhana pamodzi, Yesu anawafunsa kuti,
41 Reunidos os fariseus, interrogou-os Jesus:
42 “Kodi mukuganiza bwanji za Khristu? Ndi Mwana wa ndani?”
42 Que pensais vós do Cristo? De quem é filho? Responderam-lhe eles: De Davi.
43 Iye anawawuza kuti, “Nanga zikutheka bwanji kuti Davide poyankhula mwa Mzimu Woyera amatchula Iye ‘Ambuye?’ Pakuti akuti,
43 Replicou-lhes Jesus: Como, pois, Davi, pelo Espírito, chama-lhe Senhor, dizendo:
44 “Ambuye anati kwa Ambuye wanga:
44 Disse o Senhor ao meu Senhor: Assenta-te à minha direita, até que eu ponha os teus inimigos debaixo dos teus pés?
45 Ngati tsono Davide amamutchula ‘Ambuye,’ zingatheke bwanji kukhala mwana wake?”
45 Se Davi, pois, lhe chama Senhor, como é ele seu filho?
46 Panalibe wina anatha kuyankha, ndipo kuchokera pamenepo, panalibe wina anayerekeza kumufunsa funso.
46 E ninguém lhe podia responder palavra, nem ousou alguém, a partir daquele dia, fazer-lhe perguntas.

Ler em outra tradução

Comparar com outra

Estude este capítulo no WhatsApp

Peça à IA da Bíblia Fala para explicar Mateus 22, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.