Filemom 1

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs BKJ

Sair da comparação
1 Kuchokera kwa Paulo, amene ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu ndi Timoteyo mʼbale wathu.
1 Paulo, prisioneiro de Jesus Cristo, e Timóteo, nosso irmão, a Filemom, nosso querido e amado cooperador,
2 Kwa Apiya mlongo wathu, Arkipo msilikali mnzathu, ndiponso mpingo umene umasonkhana mʼnyumba mwanu.
2 e à nossa amada Áfia, e a Arquipo, nosso companheiro de lutas, e à igreja que está em tua casa:
3 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi inu.
3 Graça a vós e paz, da parte de Deus, nosso Pai, e da do Senhor Jesus Cristo.
4 Ine ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakukumbukira iwe mʼmapemphero anga.
4 Graças dou ao meu Deus, fazendo menção de ti sempre em minhas orações,
5 Pakuti ndamva za chikondi chako, za chikhulupiriro chako mwa Ambuye Yesu ndiponso za chikondi chako pa oyera mtima onse.
5 ouvindo o teu amor e a fé que tens para com o Senhor Jesus e para com todos os santos;
6 Ine ndikupemphera kuti mgwirizano wako ndi ife mʼchikhulupiriro ukhale opindulitsa pozamitsa nzeru zako zozindikira zinthu zilizonse zabwino zimene timagawana chifukwa cha Khristu.
6 para que a comunicação da tua fé seja eficaz, no conhecimento de toda boa coisa que há em vós, por Cristo Jesus,
7 Mʼbale, chikondi chako chandipatsa chimwemwe chachikulu ndi chilimbikitso, chifukwa umatsitsimutsa mitima ya anthu a Ambuye.
7 porque temos grande alegria e consolação no teu amor, porque por ti, ó irmão, as entranhas dos santos são revigoradas.
8 Tsopano ngakhale kuti mwa Khristu nditha kulimba mtima ndi kulamulira kuti uchite zimene uyenera kuchita,
8 Pelo que, ainda que seja muito corajoso em Cristo para te mandar o que é conveniente,
9 komabe ndikupempha mwachikondi. Ine Paulo, munthu wokalamba, ndipo tsopano ndili mʼndende chifukwa cha Khristu Yesu,
9 contudo, por amor, peço-te, sendo eu tal como sou, Paulo, o velho e agora também prisioneiro de Jesus Cristo.
10 ndikukupempha chifukwa cha mwana wanga Onesimo, amene ndamubala ndili mu unyolo.
10 Peço-te por meu filho Onésimo, que gerei nas minhas prisões,
11 Anali wopanda phindu kwa iwe, koma tsopano wasanduka wa phindu kwa iwe ndi kwa inenso.
11 o qual, noutro tempo, te foi inútil, mas, agora, muito útil a ti e a mim,
12 Ine ndikumutumizanso kwa iwe tsopano, koma potero ndikukhala ngati ndikutumiza mtima wanga weniweni.
12 e que te envio de volta; tu, portanto, torna a recebê-lo como às minhas próprias entranhas.
13 Ndikanakonda ndikanakhala naye kuno kuti iyeyo azinditumikira mʼmalo mwako pamene ndili mu unyolo chifukwa cha Uthenga Wabwino.
13 Eu bem o quisera reter comigo, para que, em teu nome, me servisse nas prisões do evangelho;
14 Koma sindikufuna kuchita kanthu osakufunsa, nʼcholinga chakuti chilichonse chabwino ungandichitire chikhale mwakufuna kwako osati mokakamiza.
14 mas sem o teu parecer, nada quis fazer, para que o teu benefício não fosse como por necessidade, mas voluntário.
15 Mwina chifukwa chimene unasiyana naye kwa kanthawi ndi chakuti ukhale nayenso nthawi zonse.
15 Porque bem pode ser que ele tenha se apartado de ti por algum tempo, para que o recebesses para sempre,
16 Osati ngati kapolo, koma woposa kapolo, ngati mʼbale wokondedwa. Iyeyu ndi wokondedwa kwambiri kwa ine koma kwa iweyo ndi wokondedwa koposa, ngati munthu komanso ngati mʼbale mwa Ambuye.
16 não já como um servo, mas além de um servo, como irmão amado, especialmente para mim e quanto mais para ti, assim na carne como no Senhor.
17 Tsono ngati umati ndine mnzako, umulandire iyeyu monga momwe ukanandilandirira ineyo.
17 Assim, pois, se me tens por companheiro, recebe-o como a mim mesmo.
18 Ngati anakulakwira kapena kukongola kanthu kalikonse, ndidzalipira ineyo.
18 E, se te fez algum mal ou te deve alguma coisa, põe isso na minha conta.
19 Ine, Paulo ndikulemba zimenezi ndi dzanja langa. Ine ndidzalipira. Nʼkosafunika kukukumbutsa kuti iweyo ngongole yako kwa ine ndi moyo wakowo.
19 Eu, Paulo, de minha própria mão o escrevi: Eu o pagarei, para não te dizer que tu mesmo te deves inteiramente a mim.
20 Mʼbale, ndikufuna kuti ndipindule nawe mwa Ambuye; tsono tsitsimutsa mtima wanga mwa Khristu.
20 Sim, irmão, eu me alegrarei de ti no Senhor; revigora as minhas entranhas no Senhor.
21 Ine ndili ndi chitsimikizo cha kumvera kwako pamene ndikukulembera kalatayi. Ndikulemba ndikudziwa kuti udzachita ngakhale kuposa zimene ndakupemphazi.
21 Confiado na tua obediência te escrevi, sabendo que ainda farás mais do que digo.
22 Chinthu chinanso ndi ichi: undikonzere malo, chifukwa ndikukhulupirira kuti Mulungu adzamvera mapemphero anu ndi kundibwezera kwa inu.
22 E além disso, prepara-me também pousada, porque confio que, pelas vossas orações, vos serei restituído.
23 Epafra, wamʼndende mnzanga chifukwa cha Khristu Yesu akupereka moni.
23 Saúdam-te Epafras, meu companheiro de prisão em Cristo Jesus,
24 Atumiki anzanga awa, Marko, Aristariko, Dema ndi Luka, akuperekanso moni.
24 Marcos, Aristarco, Demas e Lucas, meus cooperadores.
25 Chisomo cha Ambuye Yesu Khristu chikhale ndi mzimu wako.
25 A graça de nosso Senhor Jesus Cristo seja com o vosso espírito. Amém.

Ler em outra tradução

Comparar com outra

Estude este capítulo no WhatsApp

Peça à IA da Bíblia Fala para explicar Filemom 1, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.