Levítico 2

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs NTLH

Sair da comparação
NTLH Nova Tradução na Linguagem de Hoje 2000
1 “ ‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani,
1 Quando um homem oferecer cereais ao Senhor Deus, deverá moer o cereal, tirando dele a melhor farinha. Depois de misturar azeite e incenso na farinha,
2 ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova.
2 ele a entregará aos sacerdotes, que são descendentes de Arão. Um dos sacerdotes pegará um punhado da farinha com o azeite e o incenso e o queimará no altar para lembrar que a oferta toda é dada a Deus. É uma oferta de alimento que tem um cheiro agradável ao Senhor .
3 Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
3 O resto da oferta de cereais é dos sacerdotes, que são descendentes de Arão; é a parte mais sagrada, pois foi tirada da oferta dada a Deus, o Senhor .
4 “ ‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta.
4 Se a oferta de cereais forem pães assados no forno, eles deverão ser feitos da melhor farinha, mas sem fermento. Os pães podem ser grandes, feitos de farinha misturada com azeite, ou então pequenos e achatados, passando-se um pouco de azeite por cima.
5 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta.
5 Se a oferta forem pães assados na grelha, eles deverão ser feitos de farinha misturada com azeite, mas sem fermento.
6 Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya.
6 Quando fizer a oferta, o homem deverá partir o pão em pedaços e derramar azeite em cima.
7 Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
7 Se a oferta forem pães assados na frigideira, eles deverão ser feitos de farinha misturada com azeite.
8 Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa.
8 Apresente a Deus, o Senhor , essas ofertas de cereais; entregue ao sacerdote, e ele as levará ao altar.
9 Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova.
9 Ele pegará uma pequena parte da oferta e a queimará no altar para lembrar que a oferta toda é dada a Deus. É uma oferta de alimento que tem um cheiro agradável ao Senhor .
10 Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
10 O resto da oferta de cereais é dos sacerdotes, que são descendentes de Arão; é a parte mais sagrada, pois foi tirada da oferta dada a Deus, o Senhor .
11 “ ‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi.
11 Nenhuma oferta de cereais será preparada com fermento; nem fermento nem mel deverão ser usados em nenhuma oferta apresentada a Deus, o Senhor .
12 Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova.
12 Ofereça ao Senhor os cereais que forem colhidos primeiro; mas essa oferta não será queimada no altar.
13 Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.
13 Tempere com sal todas as ofertas de cereais, pois o sal representa a aliança que Deus fez com o seu povo. Toda oferta de cereais deverá ser temperada com sal.
14 “ ‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha.
14 Quando a primeira parte da colheita de cereais for oferecida a Deus, o Senhor , leve grãos de espigas verdes, esmagados e torrados no fogo.
15 Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya.
15 Ponha azeite e incenso em cima dessa oferta.
16 Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
16 Aí o sacerdote queimará no altar uma parte dessa oferta de cereais, junto com o azeite e o incenso, para lembrar que a oferta toda é dada a Deus, o Senhor .

Ler em outra tradução

Comparar com outra

Estude este capítulo no WhatsApp

Peça à IA da Bíblia Fala para explicar Levítico 2, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.