Levítico 11
Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs BKJ
1 Yehova anayankhula ndi Mose ndi Aaroni kuti,
1 E o SENHOR falou a Moisés e a Arão, dizendo-lhes:
2 “Awuze Aisraeli kuti, ‘Nyama zomwe mukhoza kudya mwa nyama zonse za dziko lapansi ndi izi:
2 Falai aos filhos de Israel, dizendo: estes são os animais que comereis entre todos os animais que estão sobre a terra:
3 Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
3 Tudo o que tem unhas fendidas, e cuja fenda das unhas se divide em duas, e rumina, entre os animais, aquilo comereis.
4 “ ‘Koma pali nyama zina zimene zimabzikula kokha kapena ndi zogawikana zipondero zimene simukuyenera kudya. Nyama zimenezi ndi ngamira, ngakhale imabzikula ilibe zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
4 Todavia, não comereis dos que ruminam, ou dos que têm unhas fendidas: como o camelo, porque rumina, mas não tem unhas fendidas; este vos será impuro;
5 Ina ndi mbira, ngakhale imabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
5 e o coelho, porque rumina, mas não tem as unhas fendidas; este vos será impuro;
6 Inanso ndi kalulu, ngakhale amabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi wodetsedwa, musadye.
6 e a lebre, porque rumina, mas não tem as unhas fendidas; esta vos será impura.
7 Nkhumba simabzikula ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
7 E o suíno, embora tenha unhas fendidas, e a fenda das unhas se divida em duas, ele não rumina; este vos será impuro;
8 Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa chifukwa ndi yodetsedwa.
8 da sua carne não comereis, nem tocareis a sua carcaça; estes vos serão impuros.
9 “ ‘Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi a mʼnyanja ndi a mʼmitsinje mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
9 Isto comereis de tudo o que está nas águas: tudo o que tem barbatanas e escamas nas águas, nos mares e nos rios; aquilo comereis.
10 Koma zamoyo zonse za mʼnyanja kapena za mʼmitsinje zimene zilibe minga ya pa msana ndi mamba, kaya ndi tizirombo tonse ta mʼmadzi ndi zamoyo zonse zopezeka mʼmenemo ndi zodetsedwa kwa inu.
10 E tudo o que não tem barbatanas nem escamas, nos mares e nos rios, tudo o que se move nas águas, e qualquer vida que está nas águas, estes serão abominação para vós.
11 Pakuti zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu, nyama yake musadye, ndipo zikafa zikhalebe zodetsedwa kwa inu.
11 Eles serão uma abominação para vós; não comereis da sua carne, porém tereis suas carcaças como abominação.
12 Chamoyo chilichonse cha mʼmadzi chimene chilibe minga ya pa msana kapena mamba ndi chodetsedwa kwa inu.
12 Tudo o que não tem barbatanas ou escamas nas águas será uma abominação para vós.
13 “ ‘Mbalame zimene simukuyenera kudya chifukwa ndi zodetsedwa ndi izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
13 E estas são as que abominareis entre as aves; não serão consumidas; são uma abominação: a águia, e o quebrantosso, e o xofrango,
14 nankapakapa, akamtema a mitundu yonse,
14 e o falcão, e o papagaio segundo a sua espécie;
15 akhungubwi a mitundu yonse,
15 todo corvo segundo a sua espécie,
16 kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo ndi mtundu uliwonse wa akabawi
16 e a coruja, e o falcão da noite, e o cuco, e o gavião segundo a sua espécie,
17 kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
17 e a pequena coruja, e o corvo-marinho, e a grande coruja,
18 tsekwe, vuwo, dembo,
18 e o cisne, e o pelicano, e o alcatraz,
19 indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
19 e a cegonha, e a garça segundo a sua espécie, e a poupa, e o morcego.
20 “ ‘Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa.
20 Todo o inseto que voa, que anda de quatro, será uma abominação para vós.
21 Komabe mwa zowuluka zokhala ndi miyendo inayi zimene mukhoza kudya ndi zokhazo zimene zili ndi miyendo yolumphira.
21 Contudo estes podereis comer de todo inseto que rasteja e voa, que anda de quatro: o que tiver pernas sobre os seus pés, para saltar com elas sobre a terra;
22 Pa zimenezo mungathe kudya izi: dzombe la mitundu yonse, atsokonombwe a mitundu yonse, nkhululu za mitundu yonse, ndi ziwala za mitundu yonse.
22 esses podereis comer: a locusta segundo a sua espécie, e a locusta lisa segundo a sua espécie, e o besouro segundo a sua espécie, e o gafanhoto segundo a sua espécie.
23 Koma za mapiko zina zonse zokhala ndi miyendo inayi muzitenge kukhala zodetsedwa kwa inu.
23 Porém todas as outras coisas rastejantes e voadoras, que tem quatro pés serão uma abominação para vós.
24 “ ‘Zimenezi zidzakudetsani. Aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
24 E por estes sereis impuros; qualquer que tocar a sua carcaça será impuro até a tarde.
25 Aliyense wonyamula chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
25 E qualquer que levar as suas carcaças lavará as suas vestes, e será impuro até a tarde.
26 “ ‘Nyama iliyonse imene ili ndi ziboda zogawikana koma mapazi ake wosagawikana, kapena imene sibzikula muyiyese yodetsedwa kwa inu ndipo munthu aliyense akakhudza nyama yakufayo, adzakhala wodetsedwa.
26 As carcaças de todo animal que tem unhas fendidas, mas a fenda não se divide em duas e que não rumina vos será por impuro; todo aquele que tocar neles será impuro.
27 Mwa nyama zonse zoyenda ndi miyendo inayi, nyama zonse zokhala ndi zikhadabo kuphazi muzitenge kukhala zodetsedwa ndipo aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
27 E tudo o que anda sobre as suas patas, entre todos os tipos de animais que andam de quatro, estes vos são impuros; qualquer que tocar sua carcaça será impuro até a tarde.
28 Aliyense wonyamula nyamazi zitafa ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu.
28 E o que levar a sua carcaça lavará as suas vestes, e será impuro até a tarde; eles vos serão por impuros.
29 “ ‘Mwa nyama zokwawa, zimene zili zodetsedwa kwa inu ndi izi: likongwe, mbewa, msambulu za mitundu yonse,
29 Estes também vos serão por impuros entre as coisas rastejantes que se arrastam sobre a terra: a doninha, e o rato, e a tartaruga segundo a sua espécie,
30 gondwa, mngʼazi, buluzi, dududu ndi nanzikambe.
30 e o ouriço, e o camaleão, e a lagartixa, e o caracol, e a toupeira.
31 Mwa nyama zonse zoyenda pansi, zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu. Munthu aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
31 Estes são impuros para vós entre tudo o que rasteja; qualquer que os tocar, estando eles mortos, será impuro até a tarde.
32 Iliyonse mwa nyama zimenezi ikafa ndi kugwera pa chiwiya chilichonse, kaya chimagwira ntchito yotani, kaya ndi chopangidwa ndi mtengo, kaya ndi cha nsalu, kaya ndi cha chikopa kapena chiguduli chiwiyacho chidzakhala chodetsedwa. Muchiviyike mʼmadzi chiwiyacho komabe chidzakhala chodetsedwa mpaka madzulo, ndipo kenaka chidzakhala choyeretsedwa.
32 Também será impuro tudo aquilo que cair sobre um destes, estando morto, seja algum vaso de madeira, ou veste, ou pele, ou saco, ou qualquer instrumento com que se faz algum trabalho, será colocado na água e será impuro até a tarde; depois, será purificado.
33 Tsono nyama ina iliyonse mwa zimenezi ikagwera mʼmbiya ya dothi, ndiye kuti chilichonse cha mʼmbiyamo chidzakhala chodetsedwa, ndipo muyenera kuswa mbiyayo.
33 E todo vaso de barro em que algum deles cair, tudo o que estiver nele será impuro; e o quebrareis.
34 Chakudya chilichonse chimene mungadye chikakhala kuti chathiridwa mʼmbiyamo, ndiye kuti chakudyacho chidzakhala chodetsedwa, ndipo madzi akumwa wochokera mʼmbiya zotere ndi wodetsedwa.
34 De todo alimento que pode ser comido, sobre o qual vier tal água será impuro; e toda bebida que se beber em tal vaso, será impura.
35 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufa chikagwera pa chinthu chilichonse kaya pa uvuni, kapena pa mʼphika, ndiye kuti zinthuzo zidzakhala zodetsedwa, ndipo ziphwanyidwe popeza ndi zodetsedwa.
35 E tudo aquilo sobre o que cair alguma parte da sua carcaça será impuro; seja o forno ou fornos para panelas, estes deverão ser quebrados porque são impuros, e serão impuros para vós.
36 Koma kasupe kapena chitsime chamadzi chidzakhala choyeretsedwa ngakhale kuti chilichonse chokhudza nyama yakufayo chidzakhala chodetsedwa. Zimenezi muzitenge kukhala zodetsedwa.
36 Porém a fonte ou cisterna, onde há muita água, será limpa; mas quem tocar na sua carcaça será impuro.
37 Chiwalo chilichonse cha nyama yakufayo chikagwera pa mbewu zimene akuti adzale, mbewu zimenezo zidzakhalabe zabwino.
37 E se alguma parte da sua carcaça cair sobre alguma semente de semear, esta será limpa;
38 Koma mbewuzo zikakhala zonyowa ndi madzi, ndipo chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo chikagwera pa mbewuzo, mbewuzo zikhale zodetsedwa kwa inu.
38 mas se alguma água for colocada sobre a semente, e alguma parte da sua carcaça cair sobre ela, vos será por impura.
39 “ ‘Ngati nyama imene mumaloledwa kudya yafa yokha, ndiye kuti aliyense wokhudza nyama yakufayo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
39 E se morrer algum animal, do qual vós podeis comer, aquele que tocar na sua carcaça será impuro até a tarde;
40 Aliyense amene adyako nyama yakufayo achape zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Aliyense amene wanyamula nyama yakufayo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
40 e aquele que comer da sua carcaça lavará as suas vestes, e será impuro até a tarde; e também quem levar a sua carcaça lavará as suas vestes, e será impuro até a tarde.
41 “ ‘Chinthu chilichonse chokwawa pansi ndi chonyansa, simuyenera kudya.
41 E cada coisa rastejante que se arrasta sobre a terra será uma abominação; isto não se comerá.
42 Musadye chilichonse chokwawa pansi, choyenda chamimba kapena choyenda ndi miyendo inayi kapenanso yambiri popeza ndi chodetsedwa.
42 Tudo o que anda sobre a barriga, e tudo o que anda de quatro, ou tudo que tem mais pés entre todas as coisas rastejantes que se arrastam sobre a terra, não comereis, porque são uma abominação.
43 Musadzisandutse nokha odetsedwa ndi chokwawa chilichonse. Musadziyipitse nazo, kuti mukhale odetsedwa.
43 Não vos façais abomináveis por nenhuma coisa rastejante que se arrasta, nem vos contamineis com eles, para não serdes contaminados por eles.
44 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, choncho dziyeretseni kuti mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera. Musadzisandutse odetsedwa ndi chokwawa chilichonse.
44 Porque eu sou o SENHOR, vosso Deus; portanto, vós vos santificareis e sereis santos, porque eu sou santo; e não contaminareis a vós mesmos com nenhum tipo de coisa rastejante que se arrasta sobre a terra.
45 Ine ndine Yehova amene ndinakutulutsani ku Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Tsono mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera.
45 Porque eu sou o SENHOR, que vos fiz sair da terra do Egito, para ser vosso Deus; portanto, vós sereis santos, porque eu sou santo.
46 “ ‘Amenewa ndi malamulo onena za nyama, mbalame, chamoyo chilichonse choyenda mʼmadzi ndiponso chamoyo chilichonse chokwawa.
46 Esta é a lei dos animais, e das aves, e de toda criatura vivente que se move nas águas, e de toda criatura que se arrasta sobre a terra,
47 Muzisiyanitsa pakati pa chodetsedwa ndi choyeretsedwa, komanso pakati pa zomwe mutha kudya ndi zomwe simuyenera kudya.’ ”
47 para fazer uma diferença entre o impuro e o limpo, e entre os animais que podem ser comidos e os animais que não podem ser comidos.
Atalhos do teclado
- Capítulo anterior←
- Próximo capítulo→
- Versículo anteriork
- Próximo versículoj
- Limpar seleçãoEsc
- Esta ajuda?
Estude este capítulo no WhatsApp
Peça à IA da Bíblia Fala para explicar Levítico 11, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.