Apocalipse 21
Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs AAI
1 Kenaka ndinaona kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano pakuti kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zinapita ndipo kunalibenso nyanja ina iliyonse.
1 “Imaibo ayu mar boubun naatu tafaram boubun aitin. Mar wantoro’ot ma’am naatu tafaram wantoro’ot ma’am etei sawar, riy auman saki iwa’an.
2 Ndinaona mzinda wopatulika, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu, utakonzedwa ngati mkwatibwi wovala zokongola kukonzekera mwamuna wake.
2 Ayu bar merar kakafiyin, Jerusalem boubun mar God biyanane tit re’er aitin, babitai tabin isan ti’abur aawan biyan baitubarin isan enan na’atube.
3 Ndipo ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Mpando Waufumu kuti, “Taonani! Malo wokhalapo Mulungu ali pakati pa anthu, ndipo Iye adzakhala ndi anthuwo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulungu mwini adzakhala nawo nakhala Mulungu wawo.
3 Naatu urama’amamaim fanan aumetawat anowar eo, ‘Boun God ana sabuw biyah i ana bar matar, naatu boro bairi hinama. I boro ana sabuw hinamatar naatu God taiyuwin boro hai God namatar bairi hinama.
4 ‘Mulungu adzapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo. Sikudzakhalanso imfa kapena kukhuza maliro kapena kulira kapena ululu popeza zakale zapita.’ ”
4 maturih nasafamen. Nati’imaim morob boro men namatar maiye’emih, o yababan o rerey o baiyababan, anayabin marasika ana sawar i earuwasair sawar.’”
5 Amene anakhala pa mpando waufumuyo anati, “Ndikulenga zinthu zonse zikhale zatsopano!” Ndipo anati, “Lemba izi, pakuti mawu awa ndi okhulupirika ndi woona.”
5 Orot nati ana urama’ama’amaim ma’am, eo, “Ayu sawar etei asinaf tibiboubuh.” Imaibo eo, “Iti inakirum nara’iy anayabin iti tur i turobe naatu karam boro hinitumatum.”
6 Iye anandiwuza kuti, “Kwatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa onse akumva ludzu, ndidzawapatsa zakumwa zaulere zochokera ku kasupe wamadzi amoyo.
6 Ayu isou eo, “Sawar etei aisawar! Ayu i An naatu Yomanin, Busurufinayan naatu Baisawarinayan. Yait sikan namamamah ayu boro yawas ana harew buruburur aurin baiyan en anitin natom.
7 Iye amene adzapambane adzalandira zonsezi, ndipo ndidzakhala Mulungu wake ndi Iye adzakhala mwana wanga.
7 Orot yait baiyow fokarin nabisnowah, i boro sawar etei ayu biyou’une nabow ayu i ana God naatu i boro ayu natu namatar.
8 Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.”
8 Baise baiwawa’irayah, baitumatum atih, eteni, asbunuwenayah, baisesebarayah, farumayah, God ana baimataren sawar kwafirenayah, naatu baifufuwenayah etei, hai efan i wairaf fora’abin in ebitakir ana kukufamaim hinara’iy na’afufurih. Nati i morob bairou’abin.”
9 Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja, anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi miliri yotsiriza isanu ndi iwiri anandiwuza kuti, “Bwera, ine ndidzakuonetsa mkwatibwi wa Mwana Wankhosa.”
9 Tounamatar seven wanawanahimaim tounamatar bai seven tew seven yomanin ana sawow kakafih yumatah ta ta bobotanen isou eo, “Kuna ayu boro Babitai boubun Lamb aawan ani’obaiy ina’itin.”
10 Ndipo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku phiri lalikulu ndi lalitali nandionetsa mzinda wopatulika, Yerusalemu ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu.
10 Naatu Anun kakafiyin matou bora’ah tounamatar eabaru airi an oyaw gagamin manin na’in tafan atit, naatu tafaram kakafiyin, Jerusalem bar merar God biyanane re nan i’obaiyu.
11 Unawala ndi ulemerero wa Mulungu, ndipo kuthwanima kwake kunali ngati mwala wamtengowapatali, ngati jasipa; woyera ngati krustalo.
11 God ana gewasin auman eargawu tafaram mamarakaw ana itinin i agim bonamanamarinabe, sawar ta woun o wair jasper na’atube, kumedarin crystal na’atube.
12 Mzindawo unali ndi mpanda waukulu ndi wautali, unali ndi zipata khumi ndi ziwiri, ndipo panali angelo khumi ndi awiri. Pa chipata chilichonse panayima mngelo. Pa chipata chilichonse panalembedwa dzina la fuko la Israeli.
12 Iti bar merar ana fur i gagamih naatu manih. Ana etawan awah etei twelve naatu tounamatar etei twelve nati awahimaim, naatu nati etawanamaim i Israel sabuw hai big twelve wabih i hikirum.
13 Kummawa kunali zipata zitatu, kumpoto zitatu, kummwera zitatu ndi kumadzulo zitatu.
13 Naatu etawan tounu i veya eyeyene hiya, etawan tounu i oyawane, tounu torene, tounu veya ere’erene.
14 Mpanda wa mzindawu unali ndi maziko khumi ndi awiri ndipo pa mazikopo panali mayina khumi ndi awiri a atumwi a Mwana Wankhosa.
14 Bar merar gagamin ana faf i twelve naatu ana wabat etei twelve tafahimaim hiwowab, nati’imaim Lamb ana tur gewasin abarayah wabih.
15 Mngelo amene ankayankhula nane uja anali ndi ndodo yagolide yoyezera mzindawo, zipata zake ndi mpanda wake.
15 Tounamatar ayu iu’uwu, umanamaim i fufunen ana isik gold bai bar merar etawan, naatu bar merar ana fur fufunen isan.
16 Mzindawo unamangidwa mofanana kutalika kwake, mulitali ndi mulifupi munali mofanana. Anayeza mzindawo ndi ndodo ija ndipo anapeza kuti mulitali, mulifupi ndi msinkhu wake kutalika kwake kunali makilomita 2,200.
16 Tounamatar re na fufun i’itin tainin rororon etei i ta’imon, ana manin naatu ana tayabar i hairi ta’imon, anayabin tainin rounane ana manin isan fufufun 2,400 kilometres. Naatu tainin roun ana tayabar isan fufufun auman i 2, 400 kilometres
17 Anayesa mpanda uja ndipo kuchindikala kwake kunali kopitirirapo mamita 65 monga mwa muyeso wa anthu umene mngelo anagwiritsa ntchito.
17 Imaibo ana faf fufun ana badowanin i’itin i at tanabat taniyab tanan etei 60 metres na’atube.
18 Mpandawo unapangidwa ndi yasipa, ndipo mzindawo unali wagolide oyengeka owala ngati galasi.
18 Bar merar ana faf i kabay wabin jasper imaim hifaf, naatu bar merar tutufin etei ana itin i goldawat, matan diridirin kiyam na’atube.
19 Maziko a mpanda wa mzindawo anali okongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali ya mtundu uliwonse. Maziko oyamba anali yasipa, achiwiri anali safiro, achitatu ndi kalikedo, achinayi ndi simaragido,
19 Bar merar ana faf an ana wabat i kabay gewasih yumatah ta ta imaim hi’abur. Ana wabat wantoro’ot i kabay wabin jasper, bairou’abin saphire, baitounin i agate, baikwafi’inin i emarod.
20 achisanu ndi sardiyo, achisanu ndi chiwiri ndi krusolito, achisanu ndi chitatu ndi berulo, achisanu ndi chinayi ndi topaziyo, a khumi ndi krusoprazo, a khumi ndi chimodzi ndi huakito, a khumi ndi chiwiri ndi emetusto.
20 bai five i onyx bai six i kanerian, bai seven karisorait, bai eight i berer, bai nine i tofas, bai ten i kalisedoni bai eleven jesinet, bai twelve ametis.
21 Zipata khumi ndi ziwiri zija zinapangidwa ndi ngale, chipata chilichonse chinapangidwa ndi ngale imodzi. Misewu ya mzindawo inali yopangidwa ndi golide oyengeka, owala ngati galasi.
21 Etawan etei twelve i kabay biyah mudid imaim hiya, naatu etawan ta’ita’imon etei i kabay biyah mudidimaim hi’abur, ef gagamin i gold akisin hirab kiyam na’atube.
22 Ine sindinaone Nyumba ya Mulungu iliyonse mu mzindawo chifukwa Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse ndi Mwana Wankhosa ndiwo Nyumba yake.
22 Bar merar gagamin wanawanan Tafaror Bar men aitin, anayabin God fairin naatu Lamb taiyuwih i Tafaror Bar.
23 Palibe chifukwa choti dzuwa kapena mwezi ziwale popeza mu mzindawo ulemerero wa Mulungu ndiwo umawalamo ndipo nyale yake ndi Mwana Wankhosa uja.
23 Bar merar men ekokok veya, o sumar tafanamaim nararan, anayabin God ana bonamanamarin marakaw ebitin, naatu Lamb i ana ramef.
24 Mitundu ya anthu idzayenda mʼkuwala kwake ndipo mafumu a dziko lapansi adzabweretsa ulemerero wawo mu mzindamo.
24 Tafaram tutufin boro i ana marakawinamaim hinaremor naatu tafaram hai aiwob boro hai guguw hinabow wanawanan hinarun.
25 Zipata zake sizidzatsekedwa ngakhale tsiku limodzi lomwe pakuti sikudzakhala usiku kumeneko.
25 Etawan awah boro mar etei bobotawiyen hina’in, boro men ta hinahir, anayabin nati’imaim boro aurin gugumin en.
26 Ulemerero ndi ulemu wa mitundu ya anthu adzapita nazo kumeneko.
26 Tafaram ana gewasin naatu ana baibifa’en sawar boro hinabow bar merar wanawanan hinarun.
27 Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa.
27 Naatu sawar men rousouwin na’atube sabuw iyabowat biya’ohow ana gubagub naatu baifufuwen ana gubagub auman tema’am boro men hinarun. Baise iyabowat wabih Lamb ana bukamaim hikikirum akisih boro hinarun.
Atalhos do teclado
- Capítulo anterior←
- Próximo capítulo→
- Versículo anteriork
- Próximo versículoj
- Limpar seleçãoEsc
- Esta ajuda?
Estude este capítulo no WhatsApp
Peça à IA da Bíblia Fala para explicar Apocalipse 21, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.