1 Timóteo 5

Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (NYA) vs BKJ

Sair da comparação
1 Usadzudzule munthu wachikulire mokalipa, koma umuchenjeze ngati abambo ako. Achinyamata uwatenge ngati abale ako.
1 Não repreendas um ancião, mas admoesta-o como a um pai; e aos jovens, como a irmãos;
2 Amayi achikulire uwatenge ngati amayi ako ndipo amayi achitsikana uwatenge ngati alongo ako, nʼkuyera mtima konse.
2 às mulheres idosas, como a mães, às jovens, como a irmãs, com toda a pureza.
3 Uziwachitira ulemu akazi amasiye amene ali okhaokha.
3 Honra as viúvas que verdadeiramente são viúvas.
4 Koma ngati mkazi wamasiye ali ndi ana ndi zidzukulu, anawo ayambe aphunzira kukwaniritsa udindo wawo pa banja lawo moopa Mulungu, potero akubweza zabwino kwa makolo awo ndi agogo awo. Pakuti zimenezi ndiye zimakondweretsa Mulungu.
4 Mas, se alguma viúva tiver filhos ou sobrinhos, aprendam eles primeiro a exercer piedade em casa, e a recompensar seus pais; porque isto é bom e aceitável diante de Deus.
5 Mkazi wamasiye amene ali yekha ndi wopanda womuthandiza, ameneyo wayika chiyembekezo chake pa Mulungu, ndipo amapemphera kosalekeza usana ndi usiku kuti Mulungu azimuthandiza.
5 Ora, a que é verdadeiramente viúva e desamparada confia em Deus e continua em súplicas e orações noite e dia;
6 Koma mkazi wamasiye amene amangokhalira kuchita zosangalatsa moyo wake, wafa kale ngakhale akanali ndi moyo.
6 mas a que vive em prazer, está morta enquanto ela vive.
7 Pereka malangizo amenewa kwa anthu kuti akhale opanda zolakwa.
7 Ordena estas coisas, para que elas sejam irrepreensíveis.
8 Ngati wina sasamalira abale ake, makamaka a mʼbanja mwake mwenimweni, ameneyo wakana chikhulupiriro ndipo ndi woyipa kuposa wosakhulupirira.
8 Contudo, se alguém não tem cuidado dos seus e principalmente dos da sua casa, negou a fé e é pior do que um infiel.
9 Mayi wamasiye aliyense amene sanakwanitse zaka 60 zakubadwa, asakhale mʼgulu la akazi amasiye. Akhale woti anakwatiwapo ndi mwamuna wake mmodzi yekha.
9 Não deixe que uma viúva seja inscrita na lista com menos de sessenta anos; tendo sido a esposa de um homem;
10 Akhale mayi woti amadziwika bwino pa ntchito zake zabwino monga kulera ana, kusamalira alendo, kusambitsa mapazi a anthu a Mulungu, kuthandiza amene ali pa mavuto ndi kudzipereka pa ntchito zonse zabwino.
10 tendo testemunho de boas obras, se criou filhos, se hospedou estranhos, se lavou os pés dos santos, se socorreu os aflitos, se diligentemente praticou toda boa obra.
11 Akazi amasiye achitsikana, usawayike mʼgulu limeneli. Pakuti zilakolako zawo zikayamba kuwavutitsa nʼkuwalekanitsa ndi Khristu, amafuna kukwatiwanso.
11 Mas recuse as viúvas mais novas, porque, quando se tornarem levianas contra Cristo, se casarão;
12 Zikatero amadziweruza okha chifukwa aphwanya lonjezo lawo loyamba.
12 tendo já a sua condenação por haverem aniquilado sua primeira fé.
13 Komanso amakhala ndi chizolowezi cha ulesi ndi kumangoyenda khomo ndi khomo. Ndipo sikungokhala aulesi kokha komanso kuchita miseche, kududukira za eni ake, kumangokamba zinthu zosayenera kukamba.
13 E, além disto, aprendem também a ser ociosas, perambulando de casa em casa; e não só ociosas, mas também paroleiras e intrometidas, falando coisas que não deviam.
14 Kotero, ndikulangiza akazi amasiye achitsikana kuti akwatiwe, akhale ndi ana, asamalire makomo awo ndipo asamupatse mdani mpata wonyoza
14 Quero, pois, que as jovens mulheres se casem, gerem filhos, governem a casa e não deem ocasião ao adversário de maldizer.
15 Akazi amasiye ena apatuka kale nʼkumatsatira Satana.
15 Porque já algumas se desviaram, indo após Satanás.
16 Ngati mayi aliyense wokhulupirira ali ndi akazi amasiye amene akuwasamalira, apitirizebe kuwasamalira ndipo asalemetse mpingo, kuti mpingo uthandize akazi amasiye amene ali okhaokha.
16 Se algum crente ou alguma crente tem viúvas, socorra-as, e não se sobrecarregue a igreja, para que possa sustentar as que de fato são viúvas.
17 Akulu ampingo amene amayangʼanira bwino zochitika za mu mpingo, ndi oyenera ulemu wowirikiza, makamaka amene ntchito yawo ndi kulalikira ndi kuphunzitsa.
17 Os anciãos que governam bem sejam dignos com dupla honra, principalmente os que trabalham na palavra e na doutrina.
18 Pakuti Mawu a Mulungu amati, “Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu,” ndi “Wantchito ngoyenera kulandira malipiro ake.”
18 Pois a Escritura diz: Não porás focinheira no boi que pisa o grão. E: O trabalhador é digno da sua remuneração.
19 Usamamvere mawu oneneza akulu ampingo pokhapokha patakhala mboni ziwiri kapena zitatu.
19 Não aceites acusação contra um ancião, senão com duas ou três testemunhas.
20 Akulu ampingo amene akuchimwa, uwadzudzule poyera kuti ena aphunzirepo.
20 Aos que pecarem, repreende-os diante de todos, para que também os outros tenham temor.
21 Ndikukulamulira pamaso pa Mulungu, pamaso pa Yesu Khristu ndi pamaso pa angelo osankhika, kuti usunge malangizowa mosachotsera ndipo usachite kalikonse mokondera.
21 Conjuro-te, diante de Deus, e do Senhor Jesus Cristo, e dos anjos eleitos, que, observem estas coisas, sem preferir um antes do outro, nada fazendo por parcialidade.
22 Usafulumire kusanjika manja munthu, ndipo usavomerezane ndi anthu ena pa machimo. Usunge bwino kuyera mtima kwako.
22 A nenhum homem imponhas precipitadamente as mãos, nem participes dos pecados alheios; conserva-te a ti mesmo puro.
23 Uleke kumangomwa madzi okha, koma uzimwako vinyo pangʼono chifukwa cha vuto lako la mʼmimba ndi kudwala kwako kwa pafupipafupi.
23 Não bebas somente água, mas usa um pouco de vinho, por causa do teu estômago e das tuas frequentes enfermidades.
24 Anthu ena machimo awo amaonekeratu poyera, amakafika pa mpando wachiweruzo eni akewo asanakafike. Machimo a anthu ena amabwera mʼmbuyo mwawo.
24 Os pecados de alguns homens são manifestos antecipadamente, precedendo o julgamento; e em alguns manifestam-se depois.
25 Momwemonso, ntchito zabwino zimaonekera poyera, ndipo ngakhale zipande kutero, sizingatheke kubisika.
25 Da mesma forma também as boas obras de alguns são manifestas antecipadamente, e as que são de outra maneira não podem ser ocultas.

Ler em outra tradução

Comparar com outra

Estude este capítulo no WhatsApp

Peça à IA da Bíblia Fala para explicar 1 Timóteo 5, comparar traduções ou montar um estudo — tudo direto pelo WhatsApp.